Yesaya 40:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya ciweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

15. Taonani, amitundu akunga dontho la m'mtsuko, nawerengedwa ngati pfumbi losalala la m'muyeso; taonani atukula zisumbu ngati kanthu kakang'ono.

16. Ndipo Lebano sakwanira kutentha, ngakhale nyama zace sizikwanira nsembe yopsereza.

17. Amitundu onse ali cabe pamaso pa Iye; awayesa ngati cinthu cacabe, ndi copanda pace,

18. Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi cithunzithunzi cotani?

Yesaya 40