Yesaya 38:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Hezekiya analoza nkhope yace kukhoma, napemphera kwa Yehova, nati,

3. Kumbukiranitu tsopano, Yehova, kuti ndayenda pamaso panu m'zoonadi ndi mtima wangwiro, ndipo ndacita zabwino pamaso panu. Ndipo Hezekiya analira kolimba.

4. Ndipo anafika mau a Yehova kwa Yesaya, ndi kuti,

5. Ukanene kwa Hezekiya, Atero Yehova, Mulungu wa Davide, kholo lako, Ndamva kupemphera kwako, ndaona misozi yako; taona, ndidzaonjezera pa masiku ako zaka khumi ndi zisanu.

6. Ndipo ndidzakupulumutsa iwe ndi mudzi uno m'manja mwa mfumu ya Asuri, ndipo ndidzacinjiriza mudzi uno.

Yesaya 38