Yesaya 34:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo mitsinjeyo idzasanduka matope akuda, ndi pfumbilo lidzasanduka suifure, ndi dziko lacelo lidzasanduka matope oyaka moto.

10. Sadzazimikai usiku, ngakhale usana; utsi wace udzakwera nthawi zonse; m'mibadwo mibadwo lidzakhala labwinja, palibe amene adzapitapo nthawi za nthawi.

11. Koma bvuo ndi nungu zidzakhalamo, ndipo kadzidzi ndi khungubwi adzakhala m'menemo, ndipo Mulungu adzatambalika pamenepo cingwe coongolera ca cisokonezo, ndi cingwe colungamitsa ciriri cosatha kucita kanthu.

12. Iwo adzaitana mfulu zace zilowe m'ufumu, koma sizidzaonekako; ndi akalonga ace onse adzakhala cabe.

13. Ndipo minga idzamera m'nyumba zace zazikuru, khwisa ndi mitungwi m'malinga mwace; ndipo adzakhala malo a ankhandwe, ndi bwalo la nthiwatiwa.

Yesaya 34