Yesaya 30:31-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Pakuti ndi mau a Yehova Asuri adzatyokatyoka, ndi ndodo yace adzammenya.

32. Ndipo nthawi zonse Yehova adze vakantha ndi ndodo yosankhikayo, padzamveka mangaka ndi zeze; ndi m'nkhondo zothunyana-thunyana, Iye adzamenyana nao.

33. Pakuti Tofeti wakonzedwa kale, inde cifukwa ca mfumu wakonzedweratu; Iye wazamitsapo, nakuzapo; mulu wacewo ndi moto ndi nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova uuyatsa ngati mtsinje wasulfure.

Yesaya 30