Yesaya 22:3-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Olamulira ako onse athawa pamodzi, anamangidwa ndi amauta; opezedwa ako onse anamangidwa pamodzi, nathawira patari.

4. Comweco ndinati, Usandiyang'ane ine, ndilira ndi kuwawa mtima; usafulumire kunditonthoza ine, cifukwa ca kufunkhidwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,

5. Pakuti ndi tsiku laphokoso, ndi lopondereza pansi, ndi lothetsa nzeru, locokera kwa Ambuye Yehova wa makamu, m'cigwa ca masomphenya, kugumuka kwa malinga, ndi kupfuulira kumapiri.

Yesaya 22