Yesaya 2:20-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Tsiku limenelo munthu adzataya ku mfuko ndi ku mileme mafano ace asiliva ndi agolidi amene anthu anampangira iye awapembedze;

21. kuti akalowe m'mapanga a m'matanthwe, ndi m'mindala a m'miyala, kuthawa kuopsya kwa Yehova, ndi ulemerero wacifumu wace, podzuka Iye kugwedeza dziko ndi mphamvu,

22. Siyani munthu, amene mpweya wace uli m'mphuno mwace; cifukwa m'mene awerengedwamo ndi muti?

Yesaya 2