Yesaya 19:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Katundu wa Aigupto.Taonani, Yehova wakwera pamwamba pa mtambo wothamanga, nadza ku Aigupto; ndi mafano a Aigupto adzagwedezeka pakufika kwace, ndi mtima wa Aigupto udzasungunuka pakati pace.

2. Ndipo ndidzapikisanitsa Aaigupto; ndipo adzamenyana wina ndi mbale wace, ndi wina ndi mnansi wace; mudzi kumenyana ndi mudzi, ndi ufumu kumenyana ndi ufumu.

3. Ndipo mzimu wa Aigupto adzakhala wacabe pakati pace; ndipo Ine ndidzaononga uphungu wace; ndimo iwo adzafunafuna mafano ndi anyanga, ndi alauli, ndi obwebweta.

4. Ndipo ndidzapereka Aigupto m'manja mwa mbuye wankharwe; ndi mfumu yaukali idzawalamulira, ati Ambuye, Yehova wa makamu.

5. Ndipo madzi adzaphwa m'nyanja yaikuru, ndipo nyanja yoyendamo madzi idzaphwa, niuma.

Yesaya 19