Yesaya 10:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. wapita pampata; wagona pa Geba, Rama anthunthumira; Gibeya wa Sauli wathawa.

30. Pfuula ndi mau ako iwe mwana wamkazi wa Galimu! tamva, iwe Laisa! iwe Anatoti wosauka!

31. Madimena ali wothawathawa; okhala m'Gebimu asonkhanakutiathawe.

32. Lero lomwe adzaima pa Nobu; agwedezera dzanja lace pa phiri la mwana wamkazi wa Ziyoni, phiri la Yerusalemu.

33. Taonani, Ambuye Yehova wa makamu adzasadza nthambi moopsya; ndipo zazitari msinkhu zidzadulidwa, ndipo zazitari zidzagwetsedwa.

34. Ndipo adzadula nkhalango za m'thengo ndi citsulo, ndipo Lebano adzagwa ndi wamphamvu.

Yesaya 10