Yeremiya 7:24-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Koma sanamvera, sanachera khutu, koma anayenda m'upo ndi m'kuuma kwa mtima wao woipa, nabwerera cambuyo osayenda m'tsogolo.

25. Ciyambire tsiku limene makolo anu anaturuka m'dziko la Aigupto kufikira lero lino, ndatumiza kwa inu atumiki anga onse, aneneri, tsiku ndi tsiku, kuuka mamawa ndi kuwatumiza iwo;

26. koma sanandimvera Ine, sanacherakhutu lao, koma anaumitsa khosi lao; anaipa koposa makolo ao.

Yeremiya 7