Yeremiya 51:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Anthu onse ali opulukira ndi opanda nzeru; wakusula golidi acitidwa manyazi ndi fanizo lace losema; pakuti fanizo lace loyenga liri bodza, mulibe mpweya m'menemo.

18. Ngwacabe, ciphamaso; nthawi yakulangidwa kwao adzatayika.

19. Gawo la Yakobo silifanafana ndi izo; pakuti Iye ndiye analenga zonse; Israyeli ndi mtundu wa colowa cace, dzina lace ndi Yehova wa makamu.

20. Iwe ndiwe cibonga canga ndi zida zanga za nkhondo; ndi iwe ndidzatyolatyola amitundu, ndi iwe ndidzaononga maufumu;

21. ndi iwe ndidzatyolatyola kavalo ndi wakwera wace;

Yeremiya 51