Yeremiya 49:35-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Yehova wa makamu atero: Taonani, ndidzatyola uta wa Elamu, ndiwo mtima wa mphamvu yao.

36. Pa Elamu ndidzatengera mphepo zinai ku mbali zinai za mlengalenga, ndidzamwaza iwo ku mphepo zonsezo; ndipo sikudzakhala mtundu kumene opitikitsidwa a Elamu sadzafikako.

37. Ndipo ndidzacititsa Elamu mantha pamaso pa amaliwongo ao, ndi pamaso pa iwo ofuna moyo wao; ndipo ndidzatengera coipa pa iwo, mkwiyo wanga waukali, ati Yehova; ndipo ndidzatumiza lupanga liwalondole, mpaka nditawatha;

38. ndipo ndidzaika mpando wacifumu wanga m'Elamu, ndipo ndidzaononga pamenepo mfumu ndi akulu, ati Yehova.

39. Koma padzaoneka masiku akutsiriza, kuti ndidzabwezanso undende wa Elamu, ati Yehova.

Yeremiya 49