30. Nanga iwe, udzacita ciani pamene udzafunkhidwa? Ngakhale udzibveka ndi zofiira, ngakhale udzibveka ndi zokometsera zagolidi, ngakhale udzikuzira maso ako ndi kupaka, udzikometsera pacabe; mabwenzi adzakunyoza adzafuna moyo wako.
31. Pakuti ndamva kubuula ngati kwa mkazi wobala, ndi msauko ngati wa mkazi wobala mwana wace woyamba, mau a mwana wamkazi wa Ziyoni wakupuma mosiyiza, wakutambasula manja ace, ndi kuti, Tsoka ine tsopano! pakuti moyo wanga walefuka cifukwa ca ambanda.