Yeremiya 36:24-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo sanaopa, sanang'ambe nsaru zao, kapena mfumu, kapena atumiki ace ali yense amene anamva mau onsewa.

25. Tsononso Elinatani ndi Deliya ndi Gemariya anapembedzera mfumu kuti asatenthe mpukutuwo; koma anakana kumvera.

26. Ndipo mfumu inauza Yeremeeli mwana wace wa mfumu, ndi Seraya mwana wa Azirieli, ndi Selemiya mwana wa Abidieli, kuti awagwire Baruki mlembi ndi Yeremiya mneneri; koma Yehova anawabisa.

Yeremiya 36