Yeremiya 22:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Musamlirire wakufa, musacite maliro ace; koma mumliritse iye amene amuka, pakuti sadzabweranso, kapena kuonanso dziko la kwao.

11. Pakuti Yehova atero za Salumu mwana wace wa Yosiya, mfumu ya Yuda, amene analamulira m'malo mwace mwa Yosiya atate wace, amene anaturuka m'malo muno: Sadzabweranso kuno nthawi iri yonse;

12. koma kumene anamtengera iye ndende, kumeneko adzafa, ndipo sadzaonanso dziko ili.

Yeremiya 22