Yeremiya 18:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,

6. Nyumba ya Israyeli inu, kodi sindingathe kucita ndi inu monga woumba uyu? ati Yehova. Taonani, monga dothi m'dzanja la woumba, momwemo inu m'dzanja langa, nyumba ya Israyeli.

7. Mphindi imene ndidzanena za mtundu wa anthu, kapena za ufumu, kuti ndizule ndi kupasula ndi kuononga;

8. ngati mtundu umene, ndaunenera, udzatembenuka kuleka coipa cao, ndidzaleka coipaco ndidati ndiwacitire.

9. Ndipo mphindi imene ndikanenera mtundu, ndi ufumu, kuti ndimangitse mudzi wace ndi kuuoka;

Yeremiya 18