Yeremiya 1:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MAU a Yeremiya mwana wa Hilikiya, wa ansembe amene anali ku Anatoti m'dziko la Benjamini;

2. amene anamdzera mau a Yehova masiku a Yosiya mwana wace wa Amoni, mfumu ya Ayuda caka cakhumi ndi citatu ca ufumu wace.

3. Anamdzeranso masiku a Yehoyakimu mwana wace wa Yosiya, mfumu ya Yuda, kufikira Zedekiya mwana wace wa Yosiya mfumu ya Yuda atatsiriza zaka khumi ndi cimodzi; kufikira a ku Yerusalemu anatengedwa ndende mwezi wacisanu.

4. Ndipo anadza kwa ine mau a Yehova, kuti,

5. Ndisanakulenge iwe m'mimba ndinakudziwa, ndipo usanabadwe ndinakupatula iwe; ndinakuika kuti ukhale mneneri wa mitundu ya anthu.

6. Ndipo ndinati, Ha, Ambuye Mulungu! taonani, sindithai kunena pakuti ndiri mwana.

Yeremiya 1