Yakobo 1:8-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. munthu wa mitima iwiri akhala wosinkhasinkha pa njira zace zonse.

9. Koma mbale woluluka adzitamandire pa ukulu wace;

10. pakuti adzapita monga duwa la udzu,

11. Pakuti laturuka dzuwa ndi kutentha kwace, ndipo laumitsa udzu; ndipo lathothoka duwa lace, ndi ukoma wa maonekedwe ace waonongeka; koteronso wacuma adzafota m'mayendedwe ace.

12. Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wabvomerezeka, adzalandira korona wa moyo, amene Ambuye adalonjezera iwo akumkonda iye.

13. Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sakhoza kuyesedwa ndi zoipa, ndipo iye mwini sayesa munthu:

14. koma munthu ali yense ayesedwa pamene cilakolako cace ca iye mwini cimkokera, nicimnyenga.

15. Pamenepo cilakolakoco citaima, cibala ucimo; ndipo ucimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

16. Musanyengedwe, abale anga okondedwa.

Yakobo 1