Oweruza 8:32-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Ndipo Gideoni mwana wa Yoasi anafa atakalamba bwino, naikidwa m'manda a Yoasi atate wace, m'Ofira wa Aabiezeri.

33. Ndipo kunali, atafa Gideoni, ana a Israyeli anabwereranso nagwadira Abaala, nayesa Baala-beriti mulungu wao.

34. Ndi ana a Israyeli sanakumbukila Yehova Mulungu wao, amene anawapulumutsa m'dzanja la adani ao onse pozungulira ponse;

35. osacitira cifundo nyumba ya Yerubaala, ndiye Gideoni, monga mwa zokoma zonse iye anacitira Israyeli.

Oweruza 8