1. Ndipo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba tsiku lomwelo ndi kuti,
2. Lemekezani YehovaPakuti atsogoleri m'Israyeli anatsogolera,Pakuti anthu anadzipereka mwaufulu.
3. Imvani mafumu inu; cherani makutu, akalonga inu;Ndidzayimbira ine Yehova, inetu;Ndidzamuyimbira nyimbo, Yehova, Mulungu wa Israyeli,
4. Yehova, muja mudaturuka m'Seiri,Muja mudayenda kucokera ku thengo la Edomu,Dziko linanjenjemera, thambo lomwe linakha,Inde mitambo inakha madzi.
5. Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,Sinai ili pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israyeli.
6. Masiku a Samagara, mwana wa Anati,Masiku a Yaeli maulendo adalekekaNdi apanjira anayenda mopazapaza,
7. Miraga idalekeka m'Israyeli, idalekeka.Mpaka ndinauka ine Debora,Ndinauka ine amai wa Israyeli.
8. Anasankha milungu yatsopano,Pamenepo nkhondo inaoneka kuzipata.Ngati cikopa kapena nthungo zidaonekaMwa zikwi makumi anai a Israyeli?