Oweruza 3:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anadzisonkanitsira ana a Amoni ndi a Amaleki, namuka nakantha Israyeli, nalanda mudzi wa m'migwalangwa nakhalamo.

14. Ndipo ana a Israyeli anatumildra Egiloni mfumu ya Moabu zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

15. Koma pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova, Yehova anawaukitsira mpulumutsi, Ehudi mwana wa Gera, Mbenjamini, munthu wamanzere, ndipo ana a Israyeli anatumiza mtulo m'dzanja lace Ikwa Egiloni mfumu ya Moabu.

16. Ndipo Ehudi anadzisulira lupanga lakuthwa konse konse utali wace mkono; nalimangirira pansi pa zobvala zace pa ncafu ya kulamanja.

17. Ndipo anapereka mtulo kwa Egiloni, mfumu ya Moabu; koma Egiloni ndiye munthu wonenepa ndithu.

Oweruza 3