Oweruza 19:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma mbuye wace ananena naye, Tisapambukire mudzi wacilendo, wosati wa ana a lsrayeli, koma tipitirire kumka ku Gibeya,

13. Nati kwa mnyamata wace, Tiyeni, tiyandikire kwinako: tigone m'Gibeya, kapena m'Rama.

14. Napitiriraiwo, nayenda, ndi dzuwa linawalowera pafupi pa Gibeya, ndiwo wa Benjamini.

15. Napambukirako, kuti alowe nagone ku Gibeya; nalowa iye, nakhala pansi m'khwalala la mudziwo, pakuti panalibe wina wowalandira m'nyumba agonemo, wakuwapatsa pogona.

16. Ndipo taonani, munthu nkhalamba anacokera ku nchito yace kumunda madzulo; munthuyu ndiye wa ku mapiri a Efraimu, nagonera ku Gibeya; kuma anthu pamenepo ndiwo Abenjamini.

17. Pamene anakweza maso ace anaona munthu wa pa ulendoyo m'khwalala la mudzi; ndi nkhalambayo inati, Umuka kuti? ufumira kuti?

Oweruza 19