Obadiya 1:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ati Yehova, Kodi sindidzaononga tsiku lija anzeru mwa Edomu, ndi luntha m'phiri la Esau?

9. Ndipo amuna anu amphamvu adzatenga nkhawa, Temani iwe, kuti onse aonongeke m'phiri la Edomu, ndi kuphedwa.

10. Cifukwa ca ciwawa unamcitira mphwako Yakobo, udzakutidwa ndi manyazi, nudzaonongeka ku nthawi yonse.

11. Tsiku lija unaima padera, tsiku lija alendo anagwira ndende makamu ace, nalowa m'zipata zace acilendo, nacitira Yerusalemu maere, iwenso unakhala ngati mmodzi wa iwowa.

Obadiya 1