Nyimbo 8:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwenzi utakhala ngati mlongwanga,Woyamwa pa bere la amai!Ndikadakupeza panja, ndikadakupsompsona;Osandinyoza munthu.

2. Ndikadakutsogolera, kukulowetsa m'nyumba ya amai,Kuti andilange mwambo; Ndikadakumwetsa vinyo wokoleretsa,Ndi madzi a makangaza anga.

3. Dzanja lamanzere lace akadanditsamiritsa kumutu,Lamanja lace ndi kundifungatira.

4. Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,Muutsiranji, mugalamutsiranji cikondi,Cisanafune mwini.

5. Ndaniyu acokera kucipululu,Alikutsamira bwenzi lace?Pa tsinde la muula ndinakugalamutsa mnyamatawe:Pomwepo amako anali mkusauka nawe,Pomwepo wakukubala anali m'pakati pa iwe.

Nyimbo 8