Nyimbo 7:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. M'kamwa mwako munge ngati vinyo woposa,Womeza tseketeke bwenzi langa,Wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.

10. Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,Ndine amene andifunayo.

11. Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda;Titsotse m'miraga.

12. Tilawire kunka ku minda yamipesa;Tiyang'ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso,Makangaza ndi kutuwa maluwa ace;Pompo ndidzakupatsa cikondi canga,

13. Mandimu anunkhira,Ndi pamakomo pathu zipatso zabwino, za mitundu mitundu, zakale ndi zatsopano,Zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.

Nyimbo 7