Numeri 8:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Pakuti a oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli ndi anga, mwa anthu ndi zoweta; tsiku lija ndinakantha oyamba kubadwa onse m'dziko la Aigupto, ndinadzipatulira iwo akhale anga.

18. Ndipo ndatenga Alevi m'malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli.

19. Ndipo ndapereka Alevi akhale mphatso ya kwa Aroni ndi ana ace amuna yocokera mwa ana a Israyeli, kucita nchito ya ana a Israyeli, m'cihema cokomanako ndi kucita cotetezera ana a Israyeli; kuti pasakhale mliri pakati pa ana a Israyeli, pakuyandikiza ana a Israyeli ku malo opatulika.

20. Ndipo Mose ndi Aroni ndi khamu lonse la ana a Israyeli anacitira Alevi monga mwa zonse Yehova adauza Mose kunena za Alevi; momwemo ana a lsrayeli anawacitira.

Numeri 8