Numeri 7:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali kuti tsiku lomwe Mose anatsiriza kumuutsa kacisi, namdzoza ndi kumpatula, ndi zipangizo zace zonse, ndi guwa la nsembe, ndi zipangizo zace zonse, nazidzoza ndi kuzipatula;

2. akalonga a Israyeli, akuru a nyumba za makolo ao, anapereka nsembe, ndiwo akalonga a mapfuko akuyang'anira owerengedwa;

3. anadza naco copereka cao pamaso pa Yehova, magareta ophimbika asanu ndi mmodzi, ndi ng'ombe khumi ndi ziwfri; akalonga awiri anapereka gareta mmodzi, ndi kalonga mmodzi ng'ombe imodzi; nabwera nazo pakhomo pa kacisi.

Numeri 7