Numeri 25:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo akufa nao mliri ndiwo zikwi makumi awiri ndi zinai.

10. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

11. Pinehasi mwana wa Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, wabweza kuzaza kwanga pa ana a Israyeli, popeza anacita nsanje ndi nsanje yanga pakati pao, kotero kuti sindinawatha ana a Israyeli m'nsanje yanga.

12. Cifukwa cace nena, Taonani, ndimpatsa iye pangano langa la mtendere;

13. ndipo lidzakhala kwa iye, ndi kwa mbeu zace zakumtsata pangano la unsembe wosatha, popeza anacita nsanje cifukwa ca Mulungu wace, anawacitira ana a Israyeli cowatetezera.

Numeri 25