9. Anaunthama, nagona pansi ngati mkango,Ngati mkango waukazi; adzamuutsa ndani?Wodalitsika ali yense wakudalitsa iwe,Wotemberereka ali yense wakutemberera iwe.
10. Pamenepo Balaki anapsa mtima pa Balamu, naomba m'manja; ndipo Balaki anati kwa Balamu, Ndinakuitana kutemberera adani ansa, ndipo unawadalitsa ndithu katatu tsopano.
11. Cifukwa cace thawira ku malo ako tsopano; ndikadakucitira ulemu waukuru; koma, taona, Yehova wakuletsera ulemu.
12. Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Kodi sindinauzanso amithenga anu amene munawatumiza kwa ine, ndi kuti,