Numeri 22:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Pamenepo mthenga wa Yehova anaima m'njira yopapatiza ya minda yampesa; mbali yina kuli linga, mbali yina linga.

25. Ndipo buru anaona mthenga wa Yehova, nadzikankhira kulinga, nakanikiza phazi la Balamu kulinga; ndipo anampandanso.

26. Pamenepo mthenga wa Yehova anapitiriranso, naima popapatiza, popanda popatukira kulamanja kapena kulamanzere.

27. Ndipo buru wace anaona mthenga wa Yehova, nagona pansi, Balamu ali pamsana pace; ndipo Balamu adapsa mtima, nampanda buru ndi ndodo.

28. Ndipo Yehova anatsegula pakamwa pace pa buru, nati uyu kwa Balamu, Ndakucitanji, kuti wandipanda katatu tsopano?

Numeri 22