Numeri 21:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Pocokapo anayenda ulendo, namanga mahema m'cigwa ca Zaredi.

13. Atacokako anayenda ulendo, namanga mahema tsidya tina la Arinoni, wokhala m'cipululu, wogwera ku malire a Aamori; popeza Arinoni ndiwo malire a Moabu, pakati pa Moabu ndi Aamori.

14. Cifukwa cace, ananena m'buku la Nkhondo za Yehova,Vahebi m'Sufa,Ndi miyendo ya Arinoni;

15. Ndi zigwa za miyendoyoZakutsikira kwao kwa Ari,Ndi kuyandikizana ndi malire a Moabu.

16. Ndipo atacokapo anamuka ku Been, ndico citsime cimene Yehova anacinena kwa Mose, Sonkhanitsa anthu, ndipo ndidzawapatsa madzi.

17. Pamenepo Israyeli anayimba nyimbo iyi:Tumphuka citsime iwe; mucithirire mang'ombe;

Numeri 21