Numeri 2:32-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Amenewo ndiwo anawerengedwa a ana a Israyeli monga mwa nyumba za makolo ao; owerengedwa onse a m'zigono, monga mwa makamu ao, ndiwo zikwi makumi khumi kasanu ndi kamodzi mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi makumi asanu.

33. Koma sanawerenga Alevi mwa ana a Israyeli; monga Yehova adauza Mose.

34. Ndipo ana a Israyeli anacita monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo anamanga mahema ao pa mbendera zao, momwemonso anayenda paulendo, yense monga mwa mabanja ace, monga mwa nyumba za makolo ace.

Numeri 2