27. Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Aseri; ndi kalonga wa ana a Aseri ndiye Pagiyeli mwana wa Okirani.
28. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai mphambu cimodzi kudza mazana asanu.
29. Ndi pfuko la Nafitali: ndi kalonga wa ana a Nafitali ndiye Ahira mwana wa Enani.
30. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.