Numeri 2:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2. Ana a Israyeli azimanga mahema ao yense ku mbendera yace, ya cizindikilo ca nyumba ya kholo lace; amange mahema ao popenyana ndi cihema cokomanako pozungulira.

3. Ndipo iwo akumanga mahema ao ku m'mawa koturuka dzuwa ndiwo a mbendera ya cigono ca Yuda, monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Yuda ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.

4. Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri, mphambu zinai, kudza mazana asanu ndi limodzi.

Numeri 2