39. Ndipo cikhale kwa inu mphonje, yakuti muziyang'anirako, ndi kukumbukila malamulo onse a Yehova, ndi kuwacita, ndi kuti musamazondazonda kutsata za m'mtima mwanu, ndi za m'maso mwanu zimene mumatsata ndi cigololo;
40. kuti mukumbukile ndi kucita malamulo anga onse, ndi kukhala wopatulikira Mulungu wanu.
41. Ine ndine Yehova Mulungu wanu, wakukuturutsani m'dziko la Aigupto, kuti ndikhale Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.