Numeri 14:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Khululukiranitu mphulupulu ya anthu awa, monga mwa cifundo canu cacikuru, ndi monga mudalekerera anthu awa, kuyambira Aigupto kufikira tsopano.

20. Ndipo Yehova anati, Ndakhululukira monga mwa mau ako:

21. koma ndithu, pali Ine, dziko lonse lapansi lidzadzazidwa ndi ulemerero wa Yehova;

22. popeza anthu onse awa amene adaona ulemerero wanga, ndi zizindikilo zanga, ndidazicita m'Aigupto ndi m'cipululu, koma anandiyesa Ine kakhumi aka, osamvera mau anga;

Numeri 14