Numeri 13:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo anakwera njira ya kumwela nafika ku Hebroni; ndi apa panali Ahimani, Sesai, ndi Talmai, ana a Anaki. (Koma atamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri ndipo anamanga Zoani m'Aigupto.)

23. Ndipo anadza ku cigwa ca Esikolo, nacekako tsango limodzi la mphesa, nalisenza awiri mopika; anabwera nazonso makangaza ndi nkhuyu.

24. Malowa anawacha cigwa ca Esikolo, cifukwa ca tsangolo ana a lsrayeli analicekako.

25. Pamenepo anabwerera atazonda dziko, atatha masiku makumi anai.

26. Ndipo anamuka, nadza kwa Mose, ndi Aroni, ndi khamu lonse la ana a Israyeli, ku cipululu ca Parana ku Kadesi; ndipo anabwezera mau iwowa, ndi khamu lonse, nawaonetsa zipatso za dzikoli.

Numeri 13