12. Munawatsogoleranso usana ndi mtambo woti njo, ndi moto tolo usiku, kuwaunikira m'njira akayendamo.
13. Munatsikiranso pa phiri la Sinai, nimunalankhula nao mocokera m'Mwamba, ndipo munawapatsa maweruzo oyenera, ndi cilamulo coona, malemba, ndi malamulo okoma;
14. ndi Sabata lanu lopatulika munawadziwitsa, nimunawalamulira malamulo, ndi malemba, ndi cilamulo, mwa dzanja la Mose mtumiki wanu;
15. ndi mkate wocokera m'mwamba munawapatsa pa njala yao; ndi madzi oturuka m'thanthwe munawaturutsira pa ludzu lao, ndi kuwauza alowe, nalandire dziko limene mudakwezapo dzanja lanu kuwapatsa.