Mlaliki 9:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndaonanso nzeru pansi pano motero, ndipo inandionekera yaikuru;

14. panali mudzi waung'ono muli anthu owerengeka; ndipo inadzako mfumu yaikuru, niizinga ndi nkhondo, nimangapo malinga akuru;

15. koma anapezedwamo mwamuna wanzeru wosauka, yemweyo napulumutsa mudziwo ndi nzeru yace; koma panalibe anthu anakumbukira wosauka ameneyo.

16. Pamenepo ndinati, Nzeru ipambana mphamvu; koma anyoza nzeru ya wosauka, osamvera mau ace.

17. Mau a anzeru acete amveka koposa kupfuula kwa wolamulira mwa zitsiru.

Mlaliki 9