Mlaliki 7:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Pakuti nzeru icinjiriza monga ndalama zicinjiriza; koma kudziwa kupambana, cifukwa nzeru isunga moyo wa eni ace.

13. Tapenya nchito ya Mulungu; pakuti ndani akhoza kulungamitsa comwe iye anacikhotetsa?

14. Tsiku la mwai kondwera, koma tsiku la tsoka lingirira; Mulungu waika ici pambali pa cinzace, kuti anthu asapeze kanthu ka m'tsogolo mwao.

Mlaliki 7