1. Samalira phazi lako popita ku nyumba ya Mulungu; pakuti kuyandikira kumvera kupambana kupereka nsembe za zitsiru; pakuti sizizindikira kuti zirikucimwa.
2. Usalankhule mwanthuku mtima wako, usafulumire kunena kanthu pamaso pa Mulungu; pakuti Mulungu ali kumwamba, iwe uli pansi; cifukwa cace mau ako akhale owerengeka.
3. Pakuti loto lafika mwakucuruka nchito; ndipo mau a citsiru mwakucuruka maneno.