1. Ponya zakudya zako pamadzi; udzazipeza popita masiku ambiri.
2. Gawira asanu ndi awiri ngakhale asanu ndi atatu; pakuti sudziwa coipa canji cidzaoneka pansi pano.
3. Mitambo ikadzala mvula, itsanulira pansi; mtengo ukagwa kumwela pena kumpoto, pomwe unagwa mtengowo udzakhala pomwepo.
4. Woyang'ana mphepo sadzafesa; ndi wopenya mitambo sadzakolola.