Miyambi 4:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.

13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14. Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.

15. Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.

16. Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.

17. Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.

Miyambi 4