Miyambi 4:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ananu, mverani mwambo wa atate,Nimuchere makutu mukadziwe luntha;

2. Pakuti ndikuphunzitsani zabwino;Musasiye cilangizo canga.

3. Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga,Wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabala wina.

4. Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine,Mtima wako uumirire mau anga;Sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

5. Tenga nzeru, tenga luntha;Usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

Miyambi 4