Miyambi 30:13-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pali mbadwo wokwezatu maso ao,Zikope zao ndi kutukula.

14. Pali mbadwo mano ao akunga malupanga, zibwano zao zikunga mipeni;Kuti adye osauka kuwacotsa kudziko, ndi aumphawi kuwacotsa mwa anthu.

15. Msundu uli ndi ana akazi awiri ati, Patsa, patsa,Pali zinthu zitatu sizikhuta konse,Ngakhale zinai sizinena, Kwatha:

16. Manda, ndi cumba,Dziko losakhuta madzi,Ndi moto wosanena, Kwatha.

17. Diso locitira atate wace ciphwete, ndi kunyoza kumvera amace,Makungubwi a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya,

18. Zinthu zitatu zindithetsa nzeru,Ngakhale zinai, sindizidziwa:

19. Njira ya mphungu m'mlengalenga,Njira ya njoka pamwala,Njira ya ngalawa pakati pa nyanja.Njira ya mwamuna ndi namwali.

20. Comweco njira ya mkazi wacigololo;Adya, napukuta pakamwa, nati, Sindinacita zoipa,

21. Cifukwa ca zinthu zitatu dziko linthunthumira;Ngakhale cifukwa ca zinai silingathe kupirira nazo:

22. Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu;Ndi citsiru citakhuta zakudya;

23. Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa;Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.

24. Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko;Koma zipambana kukhala zanzeru:

25. Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.

26. Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.

27. Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.

Miyambi 30