Miyambi 23:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.

9. Usalankhule m'makutu a wopusa;Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.

10. Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire;Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;

11. Pakuti Mombolo wao walimba;Adzawanenera mlandu wao pa iwe.

12. Lozetsa mtima wako kumwambo,Ndi makutu ako ku mau a nzeru.

13. Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.

14. Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.

15. Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;

Miyambi 23