Miyambi 23:24-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.

26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,

27. Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.

28. Pakuti abisalira ngati wacifwamba,Nacurukitsa anthu a ciwembu.

29. Ndani ali ndi cisoni? ndani asauka? ndani ali ndi makangano?Ndani ang'ung'udza? ndani alasidwa cabe? ndani afiira maso?

30. Ngamene acedwa pali vinyo,Napita kukafunafuna vinyo wosanganizidwa.

Miyambi 23