Miyambi 23:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.

14. Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.

15. Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;

16. Imso zanga zidzasangalala,Polankhula milomo yako zoongoka.

17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;

18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

Miyambi 23