Miyambi 23:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene ukhala ulinkudya ndi mkuru,Zikumbukira ameneyo ali pamaso pako;

2. Nuike mpeni pakhosi pako,Ngati uli wadyera.

3. Usakhumbe zolongosoka zace;Pokhala zakudya zonyenga.

4. Usadzitopetse kuti ulemere;Leka nzeru yako yako.

5. Kodi upenyeranji cimene kulibe?Pakuti cuma cunera mapiko,Ngati mphungu youluka mumlengalenga.

Miyambi 23