1. Pamene ukhala ulinkudya ndi mkuru,Zikumbukira ameneyo ali pamaso pako;
2. Nuike mpeni pakhosi pako,Ngati uli wadyera.
3. Usakhumbe zolongosoka zace;Pokhala zakudya zonyenga.
4. Usadzitopetse kuti ulemere;Leka nzeru yako yako.
5. Kodi upenyeranji cimene kulibe?Pakuti cuma cunera mapiko,Ngati mphungu youluka mumlengalenga.