27. Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;Koma zaka za oipa zidzafinimpha,
28. Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe;Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.
29. Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;Koma akucita zoipa adzaonongeka.
30. Wolungama sadzacotsedwa konse:Koma oipa sadzakhalabe m'dziko.