Mika 7:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kalanga ine! pakuti ndikunga atapulula zipatso za m'mwamvu, atakunkha m'munda wamphesa; palibe mphesa zakudya; moyo wanga ukhumba nkhuyu yoyamba kupsa.

2. Watha wacifundo m'dziko, palibe woongoka mwa anthu; onsewo alalira mwazi; yense asaka mbale wace ndi ukonde.

3. Manja ao onse awiri agwira coipa kucicita ndi cangu; kalonga apempha, ndi woweruza aweruza cifukwa ca mphotho; ndi wamkuruyo angonena cosakaza moyo wace; ndipo aciluka pamodzi.

Mika 7